CHINSINSI CHA MPUMULO WA KUMWAMBA

Zaka za m'mbuyo zapitazo ena anali kunenera za mtsogolo kuti posachedwa tikhala nayo nthawi ya mtambasale yambiri yomwe sitikhoza kuigwiritsa ntchito moyenera. Panali zifukwa zabwino zonenera motsimikiza motere. M'mizinda ya pa dziko lapansi lero makina a komputa akugwira ntchito yomwe ikanagwiridwa mwezi wathunthu mu mphindi zowerengeka zokha basi. Zifanizo zokhala ngati anthu zayamba kugwira ntchito zolemetsa m'malo ogwirira ntchito.

Koma ma komputa atatha kuonetsa changu chawo ndi makina ongoyenda okha anthu akhala odabwa kwambiri kusiyana ndi kale anthu nthawi yakhala ili kuwachepera masiku ano. Pamwamba pa zonse nawo mabanja nthawi ili kuwacheperabe. Abambo ndi Amayi akuona kuti nkolimba kuti apeze "Nthawi yopambana" ndi ana koma imapezeka yosakwana.

Kafukufuku adachitika m'dera lina adapeza kuti nthawi yomwe Bambo pabanja lake amakhala pamodzi ndi ana ake patsiku ndoyokwana mphindi ya masekondi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri (37 seconds) nawo mabanja akukhalanso opanda nthawi yokhalira pamodzi ndikukhudzana.

Nanga tingachitenji kuti tiyambe kukhalira pamodzi ndi kumakhudzana?

1. MANKHWALA OCHOTSERA MOYO WOTANGANIDWA

Yesu amamvetsetsa mavuto omwe amakhala ndi mabanja omwe amatanganidwa kwambiri namasowa nthawi ndipo Iye (Yesuyo) akufuna kuti timvetsetse mpumulo wauzimu omwe uli mbali ya moyo wopambana.

"Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi akutodwa ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu………phunzirani kwa Ine chifukwa ndiriwofatsa ndiwodzicepetsa mtima ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu." Mateyu 11:25,29.

Baibulo likutifotokozera kuti mpumulo wa Uzimu uwu umapezeka njira ziwiri. Kubwera kwa Khristu tsiku liri lonse kapena kubwera kwa Khristu mlungu uli wonse.


2. KULUMIKIZANA NDI YESU TSIKU LIRI LONSE

Makamu a anthu anadza kawiri kawiri ali kufuula kufuna kuti Yesu awachitire kanthu koma Khristu ananena nawo mwa mtendere ndi mwa mzimu wofatsa kwa aliyense womuzungulira Iye. Njira yotani? Anali kukhala ndi nthawi ya padera yolankhulana ndi Atate ake tsiku liri lonse. Iye anadalira pa Atate ake kosalekeza kuti apeze njira zopezera zobetchera za m'miyoyo ya anthu. (Yohane 6:57).

Ngati ife tifuna kukhala ndi moyo wopambana wokhala ngati umene Iye anakhalira tiyenera ife nthawi zonse kudalira pa Yesu - tilole Mawu Ake ndi Mzimu wake atidzaze ndi kutiumba ife. Njira yoposa yofuna kutithandiza ife pokomana nayo mivi yoyaka moto ya mdierekezi aliyense payekha ndi kutilekanitsa ndi mabanja athu ndiyo yopeza nthawi yabwino yomakomana naye Khristu, amatiuza kuti:

"KHALANI MWA INE, ndi Ine mwa inu ……. Pakuti kopanda Ine simungathe kucita kanthu. (Yohane 15:4,5) Chosowa chachikulu munthawi yathu ino,ndi njira zopezera zinthu za Uzimu zomwe zimapezeka kupyolera mu chiyanjano chathu ndi Khristu tsiku ndi tsiku".

Nsonga yopambana yomwe ifunika kutsimikizidwa yonena za chiyanjano chathu ndi Khristu ndiyo ntchito yake yomwe anaimaliza pa mtanda, kupumula koona, chitetezo chenicheni, chiyenera kukhala chifukwa cha kutsiriza kwakukulu kumene Yesu anakunena pamene Iye anafuula, pamene Iye anali kufa. "KWATHA" (Yohane 19:30) M'mawu ena. Ntchito Yake ya chiombolo idatsirizika.

"Koma tsopano (Khristu) KAMODZI PA CHITSIRIZO CHA NTHAWIZO waonekera… KUCHOTSA UCHIMO mwa nsembe ya Iye yekha". Ahebri 9:26.

Pamene Yesu anafa, "anachotsa uchimo". Ndiye chifukwa chake adanena kuti wokhulupirira amene avomereza machimo ake akhoza "kupumula" mu ntchito yomalizidwa ya Khristu. Ife tidalandiridwa.

Uchimo umapezeka titatha kusangalala kapena kumva kupweteka m'miyoyo yathu lero. Koma Yesu anathana nawo uchimo, kamodzi kwa nthawi zonse pamtanda. Kulira kwa Yesu "Kwatha", kunatsekera lonjezo lake lakuti "Ine ndidzakupumulitsani inu" ndi mawu oona. Khristu adamaliza ntchito ya chiombolo cathu pa Karivale. (Tito 2:14) kotero kuti anapumula m'manda pa Sabata nauka kuchokera m'mandamo pa tsiku loyamba la pa mlungu (Sunday) m'mawa monga WOGONJETSA uchimo ndi imfa.

Palibe china chopambana koposa kwa M'Khristu ngati mpumulo mu ntchito yake yomalizidwa ya Khristu.

"Tiyandikire ndi mtima woona M'CHIKHULUPIRIRO CHOKWANIRA …….tigwiritse chibvomerezo chosagwedera cha chiyembekezo chathu pakuti WOLONJEZAYO ALI WOKHULUPIRIKA." Aheberi 10:22,23.

Chifukwa "Wolonjezayo ali wokhulupirika" tingathe kulowa mu mpumulo wa chipulumutso umene Yesu adalonjeza. Kukhazikitsidwa, mtendere, ndi mpumulo umene timaupeza mwa Yesu tsiku liri lonse sichifukwa cha kena kali konse komwe tichita, koma ndi chifukwa cha zomwe Iye anachita pa mtanda.

Tingathe kupumula mwa Khristu chifukwa anatitsimikizira chipulumutso chathu, chitsimikizo chimenechi chimatidzutsa ife kukhala ndi Khristu tsiku liri lonse, kudya mawu Ake ndikumapuma mpweya wochokera kumwamba kupyolera mu pemphero. Kukomana kwathu ndi Yesu m'malo opemphera kumatithandiza ife kubwezedwa ku moyo wotanganidwa ndi zinthu zadziko kupita ku moyo wamtendere ndi woyera.

3. KULUMIKIZANA NDI KHRISTU MLUNGU ULI WONSE

Khristu atatha kulenga dzikoli masiku asanu ndi limodzi (Akolose 1:16,17) Anapereka tsiku la Sabata kukhala lopumula. Ndi nthawi yoikika pa mlungu uli wonse kuti ife tidzilumikizana naye Khristuyo.

"Ndipo anaziona Mulungu zonse zimene anazipanga ndipo, taonani, zinali zabwino ndithu. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi. Ndipo zinatha kupangidwa zakumwamba ndi dziko lapansi, ndi khamu lao lonse. Tsiku la chisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito yonse anaipanga; ndipo ANAPUMA tsiku lachisanu ndi chiwiri, ku ntchito yake yonse Mulungu ndipo ANADALITSA tsiku lachisanu ndi chiwiri, NALIYERETSA LIMENELO chifukwa limenelo adapuma ku ntchito yake yonse imene Mulungu anailenga ndi kupanga" - Genesis 1:31-2:1-3.

Monga Mlengi wao, Yesu "anapumula" mu Sabata yoyamba ndi Adamu ndi Hava ndipo Iye "analidalitsa" tsiku la Sabatalo ndi "Kuliyeretsa". Mulungu anapanga masiku asanu ndi awiri pa mlungu kuti adzizungulira, osati chifukwa cha phindu lake, koma chifukwa cha Adamu ndi Hava ndi kwa ifenso lero. Chifukwa Iye anawasamalira anthu awo anawalenga, Iye analinganiza kuti tsiku liri lonse la chisanu ndi chiwiri kupyolera mu miyoyo yawo yonse lidziperekedwa kumufuna Mulungu. Sabata liri lonse liyenera kumakhala lopumula kuti thupi ndi kuuzimu komwe. Kulowa kwa uchimo m'dziko lathu lino kwapangitsa kupumula pa tsiku la Sabatali kukhala kovuta.

Mpulumutsi yemwe uja adalonjeza Adamu ndi Hava "mpumulo," patatha zaka zikwi ziwiri mtsogolo mwake anaperekanso lamulo kwa Mose pa phiri la Sinai (1 Akorinto 10:1-4) Yesu anasankha mpumulo wa Sabata pakati pa Malamulo, pakati peni peni pa mtima wa Malamulo Khumi. Lamulo la chinayi limati:-

"UZIKUMBUKIRA TSIKU LA SABATA LIKHALE LOPATULIKA. Masiku asanu ndi limodzi uzigwira ndi kumaliza ntchito zako zonse, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndilo Sabata la YEHOVA Mulungu wako; usagwire ntchito iri yonse, kapena iwe wekha, kapena mwana wako wa mwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wantchito wako wamwamuna, kapena wa ntchito wako wamkazi, kapena nyama zako, kapena mlendo amene ali m'mudzi mwako, chifukwa masiku asanu ndi limodzi Yehova adamaliza zakumwamba ndi zapansi, ndi nyanja, ndi zinthu zonse ziri m'menemo, napumula tsiku la chisanu ndi chiwiri chifukwa chache Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika." Eksodo 20:8-11.

Mulungu anakhazikitsa Sabata monga tsiku "lomalikumbukira" Yehova amene "anapanga kumwamba ndi dziko lapansi" Mpumulo wa Sabata mlungu uli wonse umalumikizana ndi Mlengi yemwe anadalitsa tsiku ili nalipatula.

Pamene Yesu anali pa dziko lino lapansi Iye anapeza mwayi womalumikizana ndi Atate wake tsiku liri lonse. Iye anali kupeza mwayi kupyolera mkupumula kwake kwa pa Sabata, pomapita kukapembedza pa dzuwa la Sabata, Luka amatiuza kuti :-

"Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo TSIKU LASABATA analowa m'sunagoge, MONGA ANAZOLOWERA" - Luka 4:16.

Ngati munthu wa umulungu Yesu anafuna kumapumula pa tsiku la Sabata pamaso pa Atate Wake. Ife monga anthu a m'thupi la nyama tiyenera kumapumula koposa pamene Yesu anatsutsa miyambo yoikidwa ya a Yuda yonena za Sabata (Mateyu 12:1-12) (Yesu) anawauza kuti Mulungu anaika Sabata kuti anthu adzilumikizana ndi Iye.

"Ndipo ananena nao, Sabata linaikidwa chifukwa cha munthu, simunthu chifukwa cha Sabata; motero Mwana wa munthu ali mwini dzuwa la Sabata lomwe." - Marko 2:27, 28.

Yesu anaonetsa kufunika kwake kwa Sabata ngakhale pa imfa yake. Iye anafa tsiku lokonzekera, (Friday) "tsiku lokonzekera Sabata iri pafupi kuyamba." (Luka 23:54) Pa nthawiyo, Iye anati, "Kwatha", ndiye kuti ntchito Yake yobwera ku dziko lino lapansi kudzafera mtundu wonse wa anthu ochimwa (Mlowamalo) inatha (inamalizidwa) (Yohane 19:30 4:34; 5:30). Kukondwerera kutsirizika kwa ntchito Yake, Yesu anapumula m'manda pa tsiku lonse la Sabata.

Khristu atangotsiriza ntchito yake yakulenga patsiku lachisanu ndi chimodzi napumula tsiku lachisanu ndi chiwiri, kupyolera mu imfa Yake ya pamtanda anatsiriza ntchito Yake yakutiombola pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, napumula tsiku lachisanu ndi chiwiri.

Tsiku loyamba lapa mlungu (Sunday) anauka m'manda, Mpulumutsi wogonjetsa (Luka 24:1-7) Iye anawauza akuphunzira ake kusunga Sabata ngakhale ati adzakomane nawo mavuto atauka Iye. Polankhula za kuonongedwa kwa Yerusalemu kumene kunachitika patangotha zaka makumi anayi (40) Iye atauka kwa akufa, anawalamulira kuti :

"Ndipo pempherani kuti kuthawa kwanu kusakhale pa nyengo ya chisanu, kapena pa Sabata." - Mateyu 23:20.

Mpulumutsi wathu adafuna akuphunzira Ake ndi otembenuka kupitiriza kuchita zomwe Iye anawaphunzitsa iwo (Yohane 15:15, 16) Iye anafuna iwo kuchita nawo mpumulo wa chipulumutso ndi mpumulo wa Sabata. Iwo sanamugwiritse Iye mwala. Akuphunzira anapitiriza kusunga Sabata itatha imfa ya Yesu. (onani Luka 23:54-56; Machitidwe 13:14; 16:13; 17:2; 18:1- 4.)

Mtumwi wokodendwa, Yohane anasunga chilumikizano chake cha mlungu ndi mlungu ndi Khristu pa dzuwa la Sabata liri lonse. M'masiku ake am'tsogolo analemba chotere: Ndinagwidwa ndi Mzimu tsiku la Ambuye". (Chibvumbulutso 1:10). Molingana ndi Yesu, "Tsiku la Ambuye" ndilo tsiku la Sabata, "Pakuti Mwana wa munthu ali mwini tsiku la Sabata" Mateyu 12:8).

Pa Sabata timakondwerera zinthu ziwiri zazikulu zomwe anatsiriza Yehova m'malo mwathu: Kutilenga ndi kutipulumutsa ife. Machitachita a Sabata adzapitirira kuchitikabe kumwamba.

"Pakuti monga m'mwamba mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano limene ndidzalenga, lidzakhalabe pamaso pa Ine ati YEHOVA …… kuyambira pa Sabata lina kufikira ku linzace anthu onse adzafika kudzapembedzera pamaso pa Ine, ati YEHOVA." Yesaya 66:22, 23.

4. PHINDU LA MPUMULO WA SABATA

Anthu lero alikuponderezana wina ndi m'nzake m'miyoyo yawo. Anthu ali kutha, mabanja ali kutha kulekana. Koma Mulungu akupereka Sabata ngati njira yabwino koposa pofuna kukhala ndi moyo wabwino.

Tiyeni tione zina zomwe timapeza mu mpumulo wa Sabata:

(i) SABATA NDI CHIKUMBUTSO CHA CHILENGEDWE, PAKULISUNGA ILO KUKHALA LOPATULIKA TIMAKUMBUKIRA MLENGI WATHU. Maora ake opatulika amapereka nthawi yodabwitsa yokhudzana ndi miyoyo yathu dziko limene Mulungu adalilenga. Ndi nthawi iti yomaliza imene inu kapena banja lanu munatenga nthawi yoyenda munkhalango yokongola ya chete kapena kuyenda mbali mwa mtsinje wopita m'matanthwe? Sabata limatipatsa ife nthawi yokaona chilengedwe cha Mulungu ndikuona zodabwitsa zomwe Iye anatilengera ife.

(2) PASABATA TIMAPEZA CHIMWEMWE CHA KUPEMBEDZA NDI CHIYANJANO NDI AKHRISTU ANZATHU Pali phindu pakupembedza Mulungu ndi anzathu monga gulu lopembedza Sabata limatipatsa ife nthawi yapadera yokumana pamodzi monga thupi la mpingo kudzutsa mphamvu zathu za Uzimu.

(3) SABATA LIMAPEREKA NTHAWI YAKUCHITA NTCHITO ZOKOMA MTIMA KWA ENA. Mwina nzanu woyandikana naye wakhala ali kudwala pakati pa mlungu pamene inu munalibe nthawi yokamuona ndi kumuchezera. Pamene bwenzi limasowa wina womumvetsera mavuto ake chifukwa cha imfa ya mwamuna wake. Chifukwa chakusowa kwanu nthawi pakati pa mlungu koma mukakamuona la Sabata akakuuzani inu mavuto ake Yesu ati, "Nkololeka kuchita zabwino tsiku la Sabata." (Mateyu 12:12)

(4) SABATA NDI TSIKU LOLIMBIKITSA MABANJA Pamene Khristu analamulira kuti. "Pa Sabata, usagwire ntchito iri yonse." (Eksodo 20:10) Iye sakadapereka magwiridwe a ntchito oyenera kwa Amuna ndi Amayi osapuma pa ntchito oposa awa, Sabata ndi chim'phona choimitsa mabanja. Sabata ndi tsiku limodzi lokha m'mene tingaike m'malo motanganidwa kuikamo mapemphero, m'malo mogwira ntchito, kumangosangalala ndi kukhala mwachete. Mpumulo wa Sabata umapereka kubanja lonse nthawi yolumikizana ndi Khristu ndikupeza kwa Iye mphamvu za Uzimu.

(5) SABATA NDI NTHAWI PAMENE YESU AMABWERA PAFUPI NANU. Chiyanjano chiri chonse chimafunika kumakhala ndi nthawi yopambana yapadera, ndipo chiyanjano chathu ndi Khristu chiyeneranso kukhala nayonso nthawi yotero. Kulipereka tsiku lonse kwa Khristu mlungu uli wonse ndi njira yokha yopambana yosungira ubwenzi wathu ndi Iye kukhala wokondweretsa.

Sabata limatipatsa ife nthawi yoonjezera, yophunzira mawu a mu Baibulo, ndi nthawi yopemphera, nthawi yoonjezera yokhala wekha ndiKhristu pa malo achete ndi kumvetsera.

Yesu "anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri naliyeretsa limenelo." Ndi lonjezo lakupezeka kwake. (Genesis 2:3) Mukhoza kumvetsetsa chifukwa chake kuli kofunika kumasunga tsiku lachisanu ndi chiwiri (Saturday) lomwe liri Sabata, chifukwa ndi tsiku limene Khristu analipatula panthawi ya chilengedwe kuti alumikizane ndi ife m'njira yapadera.

Pamene Yesu analenga Sabata zimakhala ngati anali ndi maganizo ku mbadwo wathu uno. Ndi zeni-zeni zomwe tisowa mu nthawi yathu yotanganidwa yotere: Tsiku leni - leni lomwe timapuma ku kena kali konse; tsiku lopembedza Mulungu, kukhudzana ndi chilengedwe, ndi kutsimikizira pa chiyanjano m'malo mwa zinthu, SABATA.

5. KULAWA ZA MPUMULO WA KUMWAMBA

Tingathe kuwerengera phindu lonse lolumikizana ndi Yesu kupyolera mkukumana kwathu ndi Iye tsiku ndi tsiku mlungu ndi mlungu mu liwu limodzi - mpumulo. Liwu "Sabata" limachokera mu chiheberi kutanthauza mpumulo, sichodabwitsa kuti malembo amatchula tsiku lachisanu ndi chiwiri, "Sabata lakupumula" (Levitiko 23:3)

"Mulungu) pakuti wanena za tsiku la chisanu ndi chiwiri ndipo Mulungu anapumula tsiku la chisanu ndi chiwiri kuleka ntchito zake zonse; ……………..MOMWEMO UTSALIRA MPUMULO WA SABATA WA KWA ANTHU A MULUNGU …….chifukwa chake tichite changu cha kulowa mpumulowo" - Aheberi 4:4-11.

Pakuchita chita nawo mpumulo wa Sabata zimatipatsa ife kulawa mlungu ndi mlungu za chimwemwe chomwe tidzakhale nacho mu mpumulo wa kumwamba kweni-kweni.

Mpumulo umenewu si moyo wa mtambasale ai; zimatanthauza kuchinjirizidwa, mtendere ndi moyo wabwino umene ukapezeke patsinde pa moyo wambiri wosatha. Mtundu uwu wa mpumulo wa Uzimu ukhoza kuyamikiridwa kupyolera m'machita chita. Umboni wa awo amene akomana nawo machita chita a mpumulo wa chipulumutso ndi mpumulo wa Sabata. "Ngati mungalowe mumpumulo wa Yesu kupyolera mkulumikizana ndi Iye tsiku ndi tsiku, mlungu ndi mlungu mudzapeza chimwemwe choposa m'moyo wanu."

Kodi mungakonde kumuthokoza Yesu chifukwa cha mphatso yake ya mpumulo? Kodi mungakonde kumuthokoza Iye chifukwa cha lonjezano la mpumulo wa chipulumutso tsiku liri lonse pokomana ndi zobetchera za moyo ndi lonjezano la mpumulo wa Sabata mlungu uli wonse polimbikitsa chiyanjano chanu ndi Iye? Ngati simunachite choncho, kodi mungakonde kulandira chipulumutso chomwe amachipereka? Kodi mungakonde kumuuza Iye za chilako lako chanu chofuna kumasunga motere. "Inde Ambuye! Ndikufuna kupeza chimwemwe mu tsiku lomwe munalikhazikitsa." Bwanji osapanga chitsimikizo chotere tsopano lino?

 

© 2003 The Voice of Prophecy Radio Broadcast
Los Angeles, California, U.S.A.